Islamic Guide Malawi

Islamic Guide Malawi

Share

this is an islamic page the place where we advise fellow muslims islamically

10/12/2022

Assalaam alykum warahmatullah wabarakaatuh!!!!!!

Kuyamikidwa konse ndikwa Allahu Taala mafuno Abwino apite kwa mtumiki saw a kubanja kwake komanso ndi masahabah ake.

LERO TIYENI TIPHUNZIRE ZA TWAHARAH.
๐Ÿ–‹๏ธ๐Ÿ–‹๏ธ๐Ÿ–‹๏ธ๐Ÿ–‹๏ธ๐Ÿ–‹๏ธ๐Ÿ–‹๏ธ๐Ÿ–‹๏ธ๐Ÿ–‹๏ธ๐Ÿ–‹๏ธ๐Ÿ–‹๏ธ๐Ÿ–‹๏ธ

Twaharah ndi liwu la Chiarabu lomwe tanthauzo lake ndi kuyera kapena kuti Ubwino wa kusakhala ndi umve ulionse.

Ndipo Twaharah imayang'anidwa mmagawo anayiโคต๏ธ

1 Twaharah yapathupi
2 Twaharah yamuzovala
3 Twaharah yammadzi
4 Twaharah ya pamalo oswalira

Choncho mitundu imafunika kuilabadila pa nthawi yomwe tikupanga za Twahara

Mtumiki saw Adalankhula kuti,

ุฃู„ุทู‡ูˆุฑ ุดุทุฑ ุงู„ุฅูŠู…ุงู†
Ndithu ukhondi ndigawo lachikhulupiliro chachislamu.
๐ŸŒด๐ŸŒด๐ŸŒด๐ŸŒด๐ŸŒด๐ŸŒด๐ŸŒด๐ŸŒด๐ŸŒด๐ŸŒด๐ŸŒด
Komanso Mtumiki saw adalankhulanso kuti, โคต๏ธ
ุฃู„ุทู‡ูˆุฑ ู…ูุชุงุญ ุงู„ุตู„ุงุฉ
Ukhondo(kuziyeretsa) ndimakiyi aswalah

Choncho msilamu kuti akhale wa chire watayali pa ibadah akuyenera kukhala waukhondo nthawi zonse.

Nde mmene tafotokozera poyamba muja

Twaharah tikuyenera kuyang'ana mmagawo anayi amenewa.

Ungathe kukhala nditwahara yapathupi koma zovala zilibe Twaharah zikatero swalah sizingatheke.

Utha Kukhala nditwahara m'thupi ndimuzovala koma Malo oswalira ndikukhala opanda Twaharah,
Kapena tingathe kukhala oti tasamba bwinobwino komanso tachapa bwinobwino koma ndikukhala opanda Twaharah chifukwa cha madzi omwe tagwilitsa ntchito anali opanda Twaharah.................................
Ikupitilira

Pangani like kapena comment post yi kuti tidziwe kuti tikamapanga post awerengi alipo ndipo ife tudzalimbikitsika pomalembapo zambiri pa page pano

#

Want your place of worship to be the top-listed Place Of Worship in Lilongwe?
Click here to claim your Sponsored Listing.

Telephone

Address


Area 49
Lilongwe